The Madonna of the Streets
Mary's Rosaries

Home Page

Contact Us

Make a Payment, Methods of Payment, Refund and Exchange Policies

Rosaries
subpages:

How to Pray the Rosary
subpages:

Pictures Main Page
subpages:

Curriculum
subpages:

Website Terms of Use

License Agreement

Sitemap


The Work of God's Children

 Chinyanja Rosary Prayers
This language is also known as
Nyanja and Chewa.
  This language is spoken by 3,958,000 people in 
Malawi. Over 420,000 people speak this language in Mozambique.  About 1,000,000 people in Zambia and 252,000 people  in Zimbabwe speak this language.  Only about 3,000 people speak this language in Tanzania.

See also The Work of God's Children page for the illustrated version of prayers in this language.

The Sign of the Cross / Signum Crucis
+ M'DZINA LA ATATE NDI LA MWANA NDI LA MZIMU WOYERA, AMEN.

Kumvera kwa Apostoli  / The Apostles' Creed / Credo

Ine ndimvera Mulungu Atate Amphamvuzonse amene adalenga

zakumwamba ndi zapansi pano. Ndimveranso Yesu Khristu Mwana

wake yekha, Ambuye athu, amene adayikidwa m'mimba ndi mphamvu

za Mzimu Woyera nabadwa mwa Maria Virigo, adamsautsa kwa Ponsio

Pilato. Adampachika pamtanda, namwalira, adamuyika m'manda,

adalowa m'limbo ndipo mkucha wake adauka kwa akufa, adakwera

kumwamba nakhala padzanja lamanja la Mulungu Atate

Amphamvuzonse. Adzafumira komweko kudzaweruza amoyo ndi akufa.

Ndipo ndimvera Mzimu Woyera, Eklezia Katolika Woyera, ndimveranso

kuti Oyera ayanjana, Mulungu atikhululukira machimo, thupi lidzauka,

ulipo moyo osatha. Amen.


Atate Athu /  Our Father / Pater Noster
Atate athu, muli mwamba,
Dzina lanu liyeretsedwe.
Ufumu wanu udze.
Kufuna kwanu kucitidwe,
Monga kumwamba choncho pansi pano.
Mutipatse lero chakudya chathu chalero.
Mutikhululukire zochimwa zathu.
Monga ifenso tikhululukira adani athu.
Musatisiye ife muchinyengo.
Koma mutipulumutse ife kwa zoyipa.
Amen.


Another version of
Atate Athu / Our Father / Pater Noster

Atate athu muli m'mwamba, dzina lanu
liyeretsedwe, ufumu wanu udze, kufuna kwanu
kuchitidwe, monga kumwamba choncho pansi pano.
Mutipatse ife lero chakudya chathu cha lero.
Mutikhululukire ife zochimwa zathu monga
ifenso tiwakhululukira adani
athu, musatisiye ife m'chinyengo koma mutipulumutse ife ku zoyipa. Amen.


Tinione Maria / Hail Mary / Ave Maria

Tinione Maria,
wa caulere codzaza,
Ambuye ali
nanu, ndinu wodala
kupambana akazi
onse, ndipo ngodala'nso
Mwana wanu Yesu.
Maria Woyera, Amai a
Mulungu,
mutipemperere ife
ampulupulu, tsopano
ndipo'nso pa ntawi
ya kufa kwatu. Amen.


Another version of
Tinione Maria / Hail Mary / Ave Maria
Tinione Maria,
Wachaulere chodzaza,
Ambuye ali nanu.
Ndinu wodala mwa akazi onse
Wodalanso ndi mwana wanu Yesu.
Maria oyera,
Amayi a Mulungu,
Mutipempherere ife ochimwa
Tsopano ndi panthawi yakufa kwathu.
Amen.

Another version of
Tikuoneni Maria / Hail Mary
 
Tikuoneni Maria wa chaulele chodzadza,
Ambuye ali nanu.
Ndinu odala mwa akazi onse,
Ngodalanso mwana wanu Yesu.
Maria oyera amayi a mulungu
mutipempherere ife,
Tsopano ndi pa nthawi zosatha.
Amen.

Another version of
Tikuoneni Maria / Hail Mary / Ave Maria
Tikuoneni Maria wa chaulere chodzaza
Ambuye ali nanu, ndinu
wodala mwa akazi onse
ndipo ngodalanso
Mwana wanu Yesu.
Maria woyera Amayi a Mulungu
mutipempherere ife ochimwa, tsopano ndiponso pa nthawi ya kufa kwathu Amen.

Tiomone Maria / Hail Mary / Ave Maria
Tiomone Maria, wa chaulere chodzaza, Ambuye ali manu, ndimu ncwodala kopambana akagi onje ndipo ngwodalarso muana wanu Jesu.

Maria oyera amai a mulungu mutipemphere ife tsopano ndi ponjo pa nthawi ya kufa kwathu. Amen.



Malamulo a Mulungu  / The Ten Commandments

Usapembedze Mulungu wina koma ine ndekha.

Usatchule pachabe dzina la Ambuye Mulungu wako.

Udzikumbikira kuyeretsa tsiku lamulungu.

Lemekeza atate ako ndi amayi ako.

Usaphe.

Usachite chigololo.

Usabe.

Usachite umboni onama.

Usasirire ukwati wamwini.

Usachite kaduka ndi zinthu zamwini.

Ulemu Kwa Mulungu Kumwamba / Glory to God in the Highest / Gloria

Ulemu kwa Mulungu kumwamba, ndipo pansi pano

mtendere kwa anthu chifukwa iye akuwakonda.

Tikukuyamikani, tikukutamandani, Tikukupembedzani

tikukulemekezani, tikukuthokozani chifukwa cha

ulemu wanu waukulukulu. Inu Ambuye Mulungu, Mfumu wakumwamba,

Mulungu Atate a mphamvu zonse. Inunso Ambuye Yesu Khristu,

Mwana wake mmodzi yekha, Ambuye Mulungu,

Kankhosa ka Mulungu, Mwana wa Atate,

Inu amene mumachotsa machimo a anthu, mutichitire chisoni;

Inu amene mumachotsa machimo a anthu, Mverani mapemphero athu;

Inu amene mumakhala pa dzanja lamanja la Atate mutichitire chisoni.

Poti inu nokha, Yesu Khristu, ndinu woyera; Inu nokha ndinu Ambuye,

Inu nokha ndinu wopambana ndithu, limodzi ndi Mzimu Woyera, mu ulemu wa Mulungu Atate.

 



Creative Commons License
The contents of this webpage are licensed under a Creative Commons Attribution 3.0 License.
Valid HTML 4.01 Transitional
(this is the bottom of page)